Wolemba: Pacharo F. Munthali
Halisoni adamwetulira akudzisilira pakalilore. Tindevu tonga tonde tidali njo! Pachibwano chake. Kachingwe konga chikwanje kadali ndi! Pakhosi pake. Jekete loti mbu! lidali pholipholi
“Bambo, ntenthandevu wapsya,” Adatero mkazi wandodai.
“Ndikubwera mayi,” adayankha Halisoni.
Apa malingaliro adadzala m’mutu mwa ndodai ndipo misozi idamanga ufumu mu malingaliro ake. Izi zidali chomwechi pokumbukira m’mene adavutikira kuti afike pomwe adali leropa.
Makolo a Halisoni adamwali iye ali ndi zaka zitatu pangozi ya galimoto. Izi zidapangitsa kuti adzikhala ndi agogo ake aakazi aNaphiri. Apa nkuti agogo ake aamuna atatsamilanso nkono
Koma patatha zaka zitatu, nao aNaphiri adatsikira kulichete. Ndipo mikwingwirimayi idadzetsa theng’eneng’e m’moyo wa Halisoni. Zokhomazi monga ichitira mvula ya matalala ukaukulunga mpala, zidapangitsa Halisoni kuti sukulu ayisiye mufolomu ya chiwiri.
Pang’onopang’no ngati tsokonombwe, Halisoni adapeza ntchito pakampani yowotcherera zitsulo mu tawuni ya Wakwithu.
Podziwa kuti fodya wako ndi amene ali pamphuno, Halisoni amagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Izi zidachititsa kuti adzikwezedwa maudindo pafupipafupi.
Pokhala kuti pakampanipo azungu amakondapo kwambiri, iwo akamabwerere kwao katundu wao ankasiyira Halisoni. Chifukwa cha ichi, Halisoni adakhala munthu wopata. Adali ndi galimoto komanso nyumba yolozeka ndipo samasowa kanthu pakhomo pake.
“Bambo tiyi akuziziratu kuno.” Adamukumbutsa chomwecho mkazi wake wa Halisoni.
Atathana naye kazutsayo Halisoni adauyatsa ulendo wakuntchito monga mwachizolowezi.
Kuchoka tsiku lomwe mzungu wina wake waku Kosovo adamusiyira njinga ya moto chifukwa cha luntha lake pakagwiridwe ka ntchito anthu ambiri amamuchitira dumbo.
Koma iye sadalabade, m’malo mwake adapitiriza kugwira ntchito mothetsa makhang’a. Iye amachita izi podziwa kuti kulimbikira kulibe mlowam’malo.
Iye adali ndi ntchito yowonetsetsa kuti zinthu zonse zili bwino nthawi yotsegula kapena kutseka ikafika.
Ngakhale zinthu zimayenda mwa myaa! chomwechi, padali chipsinjo chimodzi pakampanipo chomwe chimamulondalonda ngati chithuzithunzi. Chipsinjocho ndiye Chidyangu, yemwe adali wachiwiri kwa iye.
Chidyangu adali ndi mbiri osati yongododometsa komanso yoopsya. Iye pokhala munthu woti ndi wachipembezo chimodzi ndi bwana, nthawi zambiri ndi bwanayo amakhala limodzi. Mukutero chilichonse iye anganene bwanayo ankangovomereza.
Nthawi zambiri Halisoni amada nkhawa kuti mwina mutu wake utupa akamaganiza za Chidyangu.
Halisoni alichiyendere ulendo wakuntchito, ntima wake udagunda mwadzidzi. Malingaliro atsiku lotsatiralo adamufikira. Adakumbuka kuti dzulo lakero adasiira Chidyangu makiyi akuntchito pamene anadwala mwadzidzi ndipo adaweluka mofulumira. Nthawi imeneyi nkuti bwana wankulu pakampanipo atapita ku Jubeki ndipo amayembekezeredwa kubwera tsiku limeneli. Chomwe chidamuwawa kwambiri chidali choti bwana adanenetsa kuti makiyi asamasiyire aliyense kupatula bwanayo. Chidali chachidziwikire kuti bwana akamva izi akhala wokwiya kwambiri.
Patsikuli akufika kuntchito mtima wake udadayamba kugunda modetsa nkhawa ngati utuluka m’chimake. Nalo thupi lidachita tsemwe ngati mwanapiye wogwera m’chithaphwi. Nkhawa yasasimbika idamupeza Poona anthu pantchitopo ali khumakhuma ngati abongololo onamizira kufa ndipo nkhope zawo zidavala chisoni.
Halisoni adayetsetsa kufulumira poyenda koma kungwangwangwa kwa maondo ake kudamuchitira njiru. Apa adadziwiratu kuti zinthu zasolobana
“Bambo Halisoni, tafotokozani za zomwe zachitika apazi.” Adatero bwana wankulu pakampanipo. Nthawi imeneyi nkuti atangofika kumene kuchokera ku South africa. Zitseko za maofesi a pakampanipo zidali zitathyoledwa, ndipo katundu wambiri adakwangwanulidwa. Halisoni adangoima kusowa chonena ngati waphonya penate. Sadakhulupilire zomwe maso ake ankaona.
“Ndi-ndi-ndi-ndidamusiyira Chi-chi-dyangu,” adayankha mwachibwibwi, ndipo m’maso muli gwa! bwanayo adamuuza Halisoni kuti yake yawuma. Kukhala ngati kutokosola pabala ndi kamtengo pa dzino lobooka, Halisoni adauzidwa kuti katundu wake alandidwa kuti akagulitsidwe pobwezeretsa katundu yemwe wabetsa.
Halisoni adazweta mutu, ndipo chokamba chidamusowa monga momwe achitira mwana akaona kholo lake likubuula chifukwa cholumidwa ndi mavu.Adadziwa kuti Chidyangu adamuyenda pansi ndipo sadakayike. Kwa iye dziko lidachita chipidigoli. Nacho chimdima cha nzanga ali pati chidadzinga m’maso mwake ndipo sadakhulupilire zomwe zinkachitikazo. Adaona ngati kutulo.
Mwadzidzi, adagwa pansi ngati thumba la kachewere, ndipo adakomoka nthawi yomweyo.
Tuesday, June 17, 2008
Subscribe to:
Post Comments (Atom)
1 comment:
Rusyada sikişen sarışın çıtır kızların rus porno olarak yaptıkları analdan sex hikayesi ve, bakire rus kızları yer alıyor
Post a Comment